Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 31:17-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Amanga m'cuuno mwace ndi mphamvu,Nalimbitsa mikono yace,

18. Azindikira kuti malonda ace ampindulira;Nyali yace sizima usiku.

19. Agwira njinga ya thonje ndi dzanja lace,Nafumbata mtengo wace.

20. Aolowera cikhato cace osauka;Natambasulira aumphawi manja ace.

21. Saopera banja lace cipale cofewa;Pakuti banja lace lonse libvala mlangali.

22. Adzipangira zimbwi zamaangamaanga;Nabvala bafuta ndi guta woti biriwiri.

23. Mwamuna wace adziwika kubwalo,Pokhala pakati pa akuru a dziko.

24. Asoka maraya abafuta, nawagulitsa;Napereka mipango kwa wogulitsa malonda.

25. Abvala mphamvu ndi ulemu;Nangoseka nthawi ya m'tsogolo.

26. Atsegula pakamwa pace ndi nzeru,Ndipo cilangizo ca cifundo ciri pa lilime lace.

27. Ayang'anira mayendedwe a banja lace,Sadya zakudya za ulesi.

28. Anace adzanyamuka, nadzamucha wodala;Mwamuna wace namtama, nati,

29. Ana akazi ambiri anacita mwangwiro,Koma iwe uposa onsewo.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 31