Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 31:14-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Akunga zombo za malonda;Nakatenga zakudya zace kutari.

15. Aukanso kusanace,Napatsa banja lace zakudya, nagawira adzakazi ace nchito.

16. Asinkhasinkha za munda, naugula;Naoka mipesa ndi zipatso za manja ace.

17. Amanga m'cuuno mwace ndi mphamvu,Nalimbitsa mikono yace,

18. Azindikira kuti malonda ace ampindulira;Nyali yace sizima usiku.

19. Agwira njinga ya thonje ndi dzanja lace,Nafumbata mtengo wace.

20. Aolowera cikhato cace osauka;Natambasulira aumphawi manja ace.

21. Saopera banja lace cipale cofewa;Pakuti banja lace lonse libvala mlangali.

22. Adzipangira zimbwi zamaangamaanga;Nabvala bafuta ndi guta woti biriwiri.

23. Mwamuna wace adziwika kubwalo,Pokhala pakati pa akuru a dziko.

24. Asoka maraya abafuta, nawagulitsa;Napereka mipango kwa wogulitsa malonda.

25. Abvala mphamvu ndi ulemu;Nangoseka nthawi ya m'tsogolo.

26. Atsegula pakamwa pace ndi nzeru,Ndipo cilangizo ca cifundo ciri pa lilime lace.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 31