Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 31:1-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mau a Lemueli mfumu, uthenga umene amace anamphunzitsa.

2. Ciani mwananga, Ciani mwana wa mimba yanga?Ciani mwana wa zowinda zanga?

3. Musapereke mphamvu yako kwa akazi,Ngakhale kuyenda m'njira yoononga mafumu.

4. Mafumu, Lemueli, mafumu sayenera kumwa vinyo;Akalonga sayenera kunena, Cakumwa caukali ciri kuti?

5. Kuti angamwe, naiwale malamulo,Naweruze mokhota anthu onse osautsidwa.

6. Wofuna kufa umpatse cakumwa caukali,Ndi vinyo kwa owawa mtima;

7. Amwe, narwale umphawi wace, Osakumbukiranso bvuto lace.

8. Tsegula pakamwa pako, ukanenere wosalankhula,Ndi mlandu wa amasiye onse.

9. Tsegula pakamwa pako,Nuweruze molungama, nunenere osauka ndi aumphawi.

10. Mkazi wangwiro ndani angampeze?Pakuti mtengo wace uposa ngale.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 31