Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 30:6-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Usaoniezere kanthu pa mau ace,Angakudzudzule, nungatsutsidwe kuti ulikunama.

7. Zinthu ziwiri ndakupemphani,Musandimane izo ndisanamwalire:

8. Mundicotsere kutari zacabe ndi mabodza;Musandipatse umphawi, ngakhale cuma,Mundidyetse zakudya zondiyenera;

9. Ndingakhute ndi kukukanani, ndi kuti, Yehova ndani?Kapena ndingasauke ndi kuba,Ndi kuchula dzina la Mulungu wanga pacabe.

10. Usanamizire kapolo kwa mbuyace,Kuti angakutemberere nawe ndi kutsutsidwa.

11. Pali mbadwo wotemberera atate ao,Osadalitsa amao.

12. Pali mbadwo wodziyesa oyera,Koma osasamba litsilo lao.

13. Pali mbadwo wokwezatu maso ao,Zikope zao ndi kutukula.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 30