Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 30:6-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Usaoniezere kanthu pa mau ace,Angakudzudzule, nungatsutsidwe kuti ulikunama.

7. Zinthu ziwiri ndakupemphani,Musandimane izo ndisanamwalire:

8. Mundicotsere kutari zacabe ndi mabodza;Musandipatse umphawi, ngakhale cuma,Mundidyetse zakudya zondiyenera;

9. Ndingakhute ndi kukukanani, ndi kuti, Yehova ndani?Kapena ndingasauke ndi kuba,Ndi kuchula dzina la Mulungu wanga pacabe.

10. Usanamizire kapolo kwa mbuyace,Kuti angakutemberere nawe ndi kutsutsidwa.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 30