Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 30:3-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Sindinaphunzira nzeruNgakhale kudziwa Woyerayo.

4. Ndani anakwera kumwamba natsikanso?Ndani wakundika nafumbata mphepo?Ndani wamanga madzi m'maraya ace?Ndani wakhazikitsa matsiriziro onse a dziko?Dzina lace ndani? dzina la mwanace ndani? kapena udziwa.

5. Mau onse a Mulungu ali oyengeka;Ndiye cikopa ca iwo amene amkhulupirira.

6. Usaoniezere kanthu pa mau ace,Angakudzudzule, nungatsutsidwe kuti ulikunama.

7. Zinthu ziwiri ndakupemphani,Musandimane izo ndisanamwalire:

8. Mundicotsere kutari zacabe ndi mabodza;Musandipatse umphawi, ngakhale cuma,Mundidyetse zakudya zondiyenera;

9. Ndingakhute ndi kukukanani, ndi kuti, Yehova ndani?Kapena ndingasauke ndi kuba,Ndi kuchula dzina la Mulungu wanga pacabe.

10. Usanamizire kapolo kwa mbuyace,Kuti angakutemberere nawe ndi kutsutsidwa.

11. Pali mbadwo wotemberera atate ao,Osadalitsa amao.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 30