Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 30:27-33 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. Dzombe liribe mfumu,Koma lituruka lonse mabwalo mabwalo.

28. Buluzi ungamgwire m'manja,Koma ali m'nyumba za mafumu.

29. Pali zinthu zitatu ziyenda cinya cinya;Ngakhale zinai ziyenda mwaufulu:

30. Mkango umene uposa zirombo kulimba,Supambukira cinthu ciri conse;

31. Kavalo wolimba m'cuuno, ndi tonde,Ndi mfumu yokhala ndi ankhondo ace.

32. Ngati wapusa podzikweza,Ngakhale kuganizira zoipa, tagwira pakamwa.

33. Pakuti potakasa mkaka, mafuta ayengekapo;Ndi popsinja mpfuno, mwazi uturukamo;Ndi potimbikira mkwiyo ndeu ionekamo.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 30