Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 30:26-33 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. Mbira ndi mtundu wopanda mphamvu,Koma ziika nyumba zao m'matanthwe.

27. Dzombe liribe mfumu,Koma lituruka lonse mabwalo mabwalo.

28. Buluzi ungamgwire m'manja,Koma ali m'nyumba za mafumu.

29. Pali zinthu zitatu ziyenda cinya cinya;Ngakhale zinai ziyenda mwaufulu:

30. Mkango umene uposa zirombo kulimba,Supambukira cinthu ciri conse;

31. Kavalo wolimba m'cuuno, ndi tonde,Ndi mfumu yokhala ndi ankhondo ace.

32. Ngati wapusa podzikweza,Ngakhale kuganizira zoipa, tagwira pakamwa.

33. Pakuti potakasa mkaka, mafuta ayengekapo;Ndi popsinja mpfuno, mwazi uturukamo;Ndi potimbikira mkwiyo ndeu ionekamo.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 30