Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 30:24-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Ziripo zinai ziri zazing'ono padziko;Koma zipambana kukhala zanzeru:

25. Nyerere ndi mtundu wosalimba,Koma zitengeratu zakudya zao m'malimwe.

26. Mbira ndi mtundu wopanda mphamvu,Koma ziika nyumba zao m'matanthwe.

27. Dzombe liribe mfumu,Koma lituruka lonse mabwalo mabwalo.

28. Buluzi ungamgwire m'manja,Koma ali m'nyumba za mafumu.

29. Pali zinthu zitatu ziyenda cinya cinya;Ngakhale zinai ziyenda mwaufulu:

30. Mkango umene uposa zirombo kulimba,Supambukira cinthu ciri conse;

Werengani mutu wathunthu Miyambi 30