Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 30:17-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Diso locitira atate wace ciphwete, ndi kunyoza kumvera amace,Makungubwi a kumtsinje adzalikolowola, ana a mphungu adzalidya,

18. Zinthu zitatu zindithetsa nzeru,Ngakhale zinai, sindizidziwa:

19. Njira ya mphungu m'mlengalenga,Njira ya njoka pamwala,Njira ya ngalawa pakati pa nyanja.Njira ya mwamuna ndi namwali.

20. Comweco njira ya mkazi wacigololo;Adya, napukuta pakamwa, nati, Sindinacita zoipa,

21. Cifukwa ca zinthu zitatu dziko linthunthumira;Ngakhale cifukwa ca zinai silingathe kupirira nazo:

22. Cifukwa ca kapolo pamene ali mfumu;Ndi citsiru citakhuta zakudya;

23. Cifukwa ca mkazi wodedwa wokwatidwa;Ndi mdzakazi amene adzalandira colowa ca mbuyace.

24. Ziripo zinai ziri zazing'ono padziko;Koma zipambana kukhala zanzeru:

25. Nyerere ndi mtundu wosalimba,Koma zitengeratu zakudya zao m'malimwe.

26. Mbira ndi mtundu wopanda mphamvu,Koma ziika nyumba zao m'matanthwe.

27. Dzombe liribe mfumu,Koma lituruka lonse mabwalo mabwalo.

28. Buluzi ungamgwire m'manja,Koma ali m'nyumba za mafumu.

29. Pali zinthu zitatu ziyenda cinya cinya;Ngakhale zinai ziyenda mwaufulu:

Werengani mutu wathunthu Miyambi 30