Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 30:11-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Pali mbadwo wotemberera atate ao,Osadalitsa amao.

12. Pali mbadwo wodziyesa oyera,Koma osasamba litsilo lao.

13. Pali mbadwo wokwezatu maso ao,Zikope zao ndi kutukula.

14. Pali mbadwo mano ao akunga malupanga, zibwano zao zikunga mipeni;Kuti adye osauka kuwacotsa kudziko, ndi aumphawi kuwacotsa mwa anthu.

15. Msundu uli ndi ana akazi awiri ati, Patsa, patsa,Pali zinthu zitatu sizikhuta konse,Ngakhale zinai sizinena, Kwatha:

16. Manda, ndi cumba,Dziko losakhuta madzi,Ndi moto wosanena, Kwatha.

17. Diso locitira atate wace ciphwete, ndi kunyoza kumvera amace,Makungubwi a kumtsinje adzalikolowola, ana a mphungu adzalidya,

18. Zinthu zitatu zindithetsa nzeru,Ngakhale zinai, sindizidziwa:

19. Njira ya mphungu m'mlengalenga,Njira ya njoka pamwala,Njira ya ngalawa pakati pa nyanja.Njira ya mwamuna ndi namwali.

20. Comweco njira ya mkazi wacigololo;Adya, napukuta pakamwa, nati, Sindinacita zoipa,

21. Cifukwa ca zinthu zitatu dziko linthunthumira;Ngakhale cifukwa ca zinai silingathe kupirira nazo:

22. Cifukwa ca kapolo pamene ali mfumu;Ndi citsiru citakhuta zakudya;

23. Cifukwa ca mkazi wodedwa wokwatidwa;Ndi mdzakazi amene adzalandira colowa ca mbuyace.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 30