Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 29:9-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Munthu wanzeru akatsutsana ndi munthu wopusa,Ngakhale akwiya, ngakhale aseka, palibe mtendere.

10. Anthu ankhanza ada wangwiro;Koma oongoka mtima asamalira moyowace.

11. Citsiru cibvumbulutsa mkwiyo wace wonse;Koma wanzeru auletsa nautontholetsa.

12. Mkuru akamvera cinyengo,Atumuki ace onse ali oipa,

13. Waumphawi ndi wotsendereza akumana;Yehova apenyetsa maso a onse awiriwo.

14. Mfumu yolamulira osauka mwantheradi,Mpando wace udzakhazikika kufikira nthawi zonse.

15. Ntyole ndi cidzudzulo zipatsa nzeru;Koma mwana womlekerera acititsa amace manyazi.

16. Pocuruka oipa zolakwa zicuruka;Koma olungama adzaona kugwa kwao.

17. Langiza mwana wako, ndipo adzakupumitsa;Nadzasangalatsa moyo wako.

18. Popanda cibvumbulutso anthu amasauka;Koma wosunga cilamulo adalitsika.

19. Kapolo sangalangizidwe ndi mau,Pakuti azindikira koma osabvomera.

20. Kodi uona munthu wansontho m'mau ace?Ngakhale citsiru cidzacenjera, koma ameneyo ai.

21. Yemwe alera kapolo wace mwa ufulu kuyambira ubwana wace,Pambuyo pace adzadziyesa mwana wobala.

22. Mwamuna wamkwiyo aputa makangano;Waukali acuruka zolakwa.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 29