Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 29:3-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Mwamuna wokonda nzeru akondweretsa atate wace;Koma wotsagana ndi akazi adama amwaza cuma.

4. Mfumu akhazikitsa dziko ndi ciweruzo;Koma wosonkhetsa anthu mphatso alipululutsa.

5. Wosyasyalika mnzace Acherera mapazi ace ukonde.

6. M'kulakwa kwa woipa muli msampha;Koma wolungama ayimba, nakondwera.

7. Wolungama asamalira mlandu wa osauka;Koma woipa alibe nzeru yakuudziwa.

8. Anthu onyoza atentha mudzi;Koma anzeru alezetsa mkwiyo.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 29