3. Mwamuna wokonda nzeru akondweretsa atate wace;Koma wotsagana ndi akazi adama amwaza cuma.
4. Mfumu akhazikitsa dziko ndi ciweruzo;Koma wosonkhetsa anthu mphatso alipululutsa.
5. Wosyasyalika mnzace Acherera mapazi ace ukonde.
6. M'kulakwa kwa woipa muli msampha;Koma wolungama ayimba, nakondwera.
7. Wolungama asamalira mlandu wa osauka;Koma woipa alibe nzeru yakuudziwa.
8. Anthu onyoza atentha mudzi;Koma anzeru alezetsa mkwiyo.