Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 29:3-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Mwamuna wokonda nzeru akondweretsa atate wace;Koma wotsagana ndi akazi adama amwaza cuma.

4. Mfumu akhazikitsa dziko ndi ciweruzo;Koma wosonkhetsa anthu mphatso alipululutsa.

5. Wosyasyalika mnzace Acherera mapazi ace ukonde.

6. M'kulakwa kwa woipa muli msampha;Koma wolungama ayimba, nakondwera.

7. Wolungama asamalira mlandu wa osauka;Koma woipa alibe nzeru yakuudziwa.

8. Anthu onyoza atentha mudzi;Koma anzeru alezetsa mkwiyo.

9. Munthu wanzeru akatsutsana ndi munthu wopusa,Ngakhale akwiya, ngakhale aseka, palibe mtendere.

10. Anthu ankhanza ada wangwiro;Koma oongoka mtima asamalira moyowace.

11. Citsiru cibvumbulutsa mkwiyo wace wonse;Koma wanzeru auletsa nautontholetsa.

12. Mkuru akamvera cinyengo,Atumuki ace onse ali oipa,

13. Waumphawi ndi wotsendereza akumana;Yehova apenyetsa maso a onse awiriwo.

14. Mfumu yolamulira osauka mwantheradi,Mpando wace udzakhazikika kufikira nthawi zonse.

15. Ntyole ndi cidzudzulo zipatsa nzeru;Koma mwana womlekerera acititsa amace manyazi.

16. Pocuruka oipa zolakwa zicuruka;Koma olungama adzaona kugwa kwao.

17. Langiza mwana wako, ndipo adzakupumitsa;Nadzasangalatsa moyo wako.

18. Popanda cibvumbulutso anthu amasauka;Koma wosunga cilamulo adalitsika.

19. Kapolo sangalangizidwe ndi mau,Pakuti azindikira koma osabvomera.

20. Kodi uona munthu wansontho m'mau ace?Ngakhale citsiru cidzacenjera, koma ameneyo ai.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 29