Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 29:17-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Langiza mwana wako, ndipo adzakupumitsa;Nadzasangalatsa moyo wako.

18. Popanda cibvumbulutso anthu amasauka;Koma wosunga cilamulo adalitsika.

19. Kapolo sangalangizidwe ndi mau,Pakuti azindikira koma osabvomera.

20. Kodi uona munthu wansontho m'mau ace?Ngakhale citsiru cidzacenjera, koma ameneyo ai.

21. Yemwe alera kapolo wace mwa ufulu kuyambira ubwana wace,Pambuyo pace adzadziyesa mwana wobala.

22. Mwamuna wamkwiyo aputa makangano;Waukali acuruka zolakwa.

23. Kudzikuza kwa munthu kudzamcepetsa;Koma wokhala ndi mtima wodzicepetsa adzalemekezedwa.

24. Woyenda ndi mbala ada moyo wace wace;Amva kulumbira, koma osaulula kanthu.

25. Kuopa anthu kuchera msampha;Koma wokhulupirira Yehova adzapulumuka,

26. Ambiri afunafuna ciyanjano ca mkuru;Koma ciweruzo ca munthu cicokera kwa Yehova.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 29