Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 29:12-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Mkuru akamvera cinyengo,Atumuki ace onse ali oipa,

13. Waumphawi ndi wotsendereza akumana;Yehova apenyetsa maso a onse awiriwo.

14. Mfumu yolamulira osauka mwantheradi,Mpando wace udzakhazikika kufikira nthawi zonse.

15. Ntyole ndi cidzudzulo zipatsa nzeru;Koma mwana womlekerera acititsa amace manyazi.

16. Pocuruka oipa zolakwa zicuruka;Koma olungama adzaona kugwa kwao.

17. Langiza mwana wako, ndipo adzakupumitsa;Nadzasangalatsa moyo wako.

18. Popanda cibvumbulutso anthu amasauka;Koma wosunga cilamulo adalitsika.

19. Kapolo sangalangizidwe ndi mau,Pakuti azindikira koma osabvomera.

20. Kodi uona munthu wansontho m'mau ace?Ngakhale citsiru cidzacenjera, koma ameneyo ai.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 29