11. Citsiru cibvumbulutsa mkwiyo wace wonse;Koma wanzeru auletsa nautontholetsa.
12. Mkuru akamvera cinyengo,Atumuki ace onse ali oipa,
13. Waumphawi ndi wotsendereza akumana;Yehova apenyetsa maso a onse awiriwo.
14. Mfumu yolamulira osauka mwantheradi,Mpando wace udzakhazikika kufikira nthawi zonse.
15. Ntyole ndi cidzudzulo zipatsa nzeru;Koma mwana womlekerera acititsa amace manyazi.