10. Anthu ankhanza ada wangwiro;Koma oongoka mtima asamalira moyowace.
11. Citsiru cibvumbulutsa mkwiyo wace wonse;Koma wanzeru auletsa nautontholetsa.
12. Mkuru akamvera cinyengo,Atumuki ace onse ali oipa,
13. Waumphawi ndi wotsendereza akumana;Yehova apenyetsa maso a onse awiriwo.
14. Mfumu yolamulira osauka mwantheradi,Mpando wace udzakhazikika kufikira nthawi zonse.
15. Ntyole ndi cidzudzulo zipatsa nzeru;Koma mwana womlekerera acititsa amace manyazi.
16. Pocuruka oipa zolakwa zicuruka;Koma olungama adzaona kugwa kwao.
17. Langiza mwana wako, ndipo adzakupumitsa;Nadzasangalatsa moyo wako.
18. Popanda cibvumbulutso anthu amasauka;Koma wosunga cilamulo adalitsika.
19. Kapolo sangalangizidwe ndi mau,Pakuti azindikira koma osabvomera.