Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 28:9-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Wopewetsa khutu lace kuti asamve cilamulo,Ngakhale pemphero lace linyansa.

10. Wosoceretsa oongoka mtima alowe m'njira yoipa,Adzagwa mwini m'dzenje lace;Koma angwiro adzalandira colowa cabwino.

11. Wolemera adziyesa wanzeru;Koma wosauka wozindikira aululitsa zace.

12. Posekera olungama pali ulemerero wambiri;Koma pouka oipa anthu amabisala.

13. Wobisa macimo ace sadzaona mwai;Koma wakuwabvomereza, nawasiya adzacitidwa cifundo.

14. Wodala munthu wakuopakosalekeza;Koma woumitsa mtima wace adzagwa m'zoipa.

15. Monga mkango wobangula ndi cirombo coyendayenda,Momwemo mfumu yoipa ya anthu osauka.

16. Kalonga wosowa nzeru apambana kusautsa;Koma yemwe ada cisiriro adzatanimphitsa moyo wace.

17. Woparamula mlandu wakupha munthu adzathawira kudzenje;Asamuletse.

18. Woyenda mwangwiro adzapulumuka;Koma wokhota m'mayendedwe ace adzagwa posacedwa.

19. Wolima munda wace zakudya zidzamkwanira;Koma wotsata anthu opanda pace umphawi udzamkwanira.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 28