Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 28:5-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Oipa samvetsetsa ciweruzo;Koma omwe afuna Yehova amvetsetsa zonse.

6. Waumphawi woyenda mwangwiroApambana ndi yemwe akhotetsa njira zace, angakhale alemera.

7. Wosunga cilamulo ndiye mwana wozindikira;Koma mnzao wa adyera acititsa atate wace manyazi.

8. Wocurukitsa cuma cace, pokongoletsa ndi phindu,Angokundikira yemwe acitira osauka cisoni.

9. Wopewetsa khutu lace kuti asamve cilamulo,Ngakhale pemphero lace linyansa.

10. Wosoceretsa oongoka mtima alowe m'njira yoipa,Adzagwa mwini m'dzenje lace;Koma angwiro adzalandira colowa cabwino.

11. Wolemera adziyesa wanzeru;Koma wosauka wozindikira aululitsa zace.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 28