4. Omwe asiya cilamulo atama oipa;Koma omwe asunga cilamulo akangana nao.
5. Oipa samvetsetsa ciweruzo;Koma omwe afuna Yehova amvetsetsa zonse.
6. Waumphawi woyenda mwangwiroApambana ndi yemwe akhotetsa njira zace, angakhale alemera.
7. Wosunga cilamulo ndiye mwana wozindikira;Koma mnzao wa adyera acititsa atate wace manyazi.
8. Wocurukitsa cuma cace, pokongoletsa ndi phindu,Angokundikira yemwe acitira osauka cisoni.