Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 28:4-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Omwe asiya cilamulo atama oipa;Koma omwe asunga cilamulo akangana nao.

5. Oipa samvetsetsa ciweruzo;Koma omwe afuna Yehova amvetsetsa zonse.

6. Waumphawi woyenda mwangwiroApambana ndi yemwe akhotetsa njira zace, angakhale alemera.

7. Wosunga cilamulo ndiye mwana wozindikira;Koma mnzao wa adyera acititsa atate wace manyazi.

8. Wocurukitsa cuma cace, pokongoletsa ndi phindu,Angokundikira yemwe acitira osauka cisoni.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 28