Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 28:23-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Adzamkomera mtima wodzudzula m'tsogolo mwace,Koposa wosyasyalika ndi lilime lace.

24. Wobera atate wace, pena amace, nati, Palibe kulakwa;Ndiye mnzace wa munthu wopasula.

25. Wodukidwa mtima aputa makangano;Koma wokhulupirira Yehova adzakula.

26. Wokhulupirira mtima wace wace ali wopusa;Koma woyenda mwanzeru adzapulumuka,

27. Wogawira aumphawi sadzasowa;Koma wophimba maso ace adzatembereredwa kwambiri.

28. Pouka oipa anthu amabisala;Koma pakufa amenewo olungama acuruka.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 28