Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 28:21-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Cetera siliri labwino,Ngakhale kulakwa kuti ukadye kanthu.

22. Mwini diso lankhwenzule akangaza kulemera,Osadziwa kuti umphawi udzamfikira.

23. Adzamkomera mtima wodzudzula m'tsogolo mwace,Koposa wosyasyalika ndi lilime lace.

24. Wobera atate wace, pena amace, nati, Palibe kulakwa;Ndiye mnzace wa munthu wopasula.

25. Wodukidwa mtima aputa makangano;Koma wokhulupirira Yehova adzakula.

26. Wokhulupirira mtima wace wace ali wopusa;Koma woyenda mwanzeru adzapulumuka,

27. Wogawira aumphawi sadzasowa;Koma wophimba maso ace adzatembereredwa kwambiri.

28. Pouka oipa anthu amabisala;Koma pakufa amenewo olungama acuruka.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 28