2. Pocimwa dziko akalonga ace acuruka;Koma anthu ozindikira ndi odziwa alikhazikikitsa nthawi yaikuru.
3. Munthu waumphawi wotsendereza osaukaAkunga mvula yamadzi yokokolola dzinthu.
4. Omwe asiya cilamulo atama oipa;Koma omwe asunga cilamulo akangana nao.
5. Oipa samvetsetsa ciweruzo;Koma omwe afuna Yehova amvetsetsa zonse.
6. Waumphawi woyenda mwangwiroApambana ndi yemwe akhotetsa njira zace, angakhale alemera.