Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 28:16-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Kalonga wosowa nzeru apambana kusautsa;Koma yemwe ada cisiriro adzatanimphitsa moyo wace.

17. Woparamula mlandu wakupha munthu adzathawira kudzenje;Asamuletse.

18. Woyenda mwangwiro adzapulumuka;Koma wokhota m'mayendedwe ace adzagwa posacedwa.

19. Wolima munda wace zakudya zidzamkwanira;Koma wotsata anthu opanda pace umphawi udzamkwanira.

20. Munthu wokhulupirika ali ndi madalitso ambiri;Koma wokangaza kulemera sadzapulumuka cilango,

21. Cetera siliri labwino,Ngakhale kulakwa kuti ukadye kanthu.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 28