Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 28:1-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Woipaathawapalibewomthamangitsa;Koma olungama alimba mtima ngati mkango.

2. Pocimwa dziko akalonga ace acuruka;Koma anthu ozindikira ndi odziwa alikhazikikitsa nthawi yaikuru.

3. Munthu waumphawi wotsendereza osaukaAkunga mvula yamadzi yokokolola dzinthu.

4. Omwe asiya cilamulo atama oipa;Koma omwe asunga cilamulo akangana nao.

5. Oipa samvetsetsa ciweruzo;Koma omwe afuna Yehova amvetsetsa zonse.

6. Waumphawi woyenda mwangwiroApambana ndi yemwe akhotetsa njira zace, angakhale alemera.

7. Wosunga cilamulo ndiye mwana wozindikira;Koma mnzao wa adyera acititsa atate wace manyazi.

8. Wocurukitsa cuma cace, pokongoletsa ndi phindu,Angokundikira yemwe acitira osauka cisoni.

9. Wopewetsa khutu lace kuti asamve cilamulo,Ngakhale pemphero lace linyansa.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 28