Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 28:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Woipaathawapalibewomthamangitsa;Koma olungama alimba mtima ngati mkango.

2. Pocimwa dziko akalonga ace acuruka;Koma anthu ozindikira ndi odziwa alikhazikikitsa nthawi yaikuru.

3. Munthu waumphawi wotsendereza osaukaAkunga mvula yamadzi yokokolola dzinthu.

4. Omwe asiya cilamulo atama oipa;Koma omwe asunga cilamulo akangana nao.

5. Oipa samvetsetsa ciweruzo;Koma omwe afuna Yehova amvetsetsa zonse.

6. Waumphawi woyenda mwangwiroApambana ndi yemwe akhotetsa njira zace, angakhale alemera.

7. Wosunga cilamulo ndiye mwana wozindikira;Koma mnzao wa adyera acititsa atate wace manyazi.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 28