Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 27:17-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Citsulo cinola citsulo;Comweco munthu anola nkhope ya mnzace.

18. Wosunga mkuyu adzadya zipatso zace;Wosamalira ambuyace adzalemekezedwa.

19. Monga m'madzi nkhope zionana,Momwemo mitima ya anthu idziwana.

20. Kunsi kwa manda ndi kucionongeko sikukhuta;Ngakhale maso a munthu sakhutai.

21. Siliva asungunuka m'mbiya,Ndi golidi m'ng'anjo,Motero comwe munthu acitama adziwika naco.

22. Ungakhaleukonolacitsirum'mtondo ndi munsi, pamodzi ndi mphale,Koma utsiru wace sudzamcoka.

23. Udziwitsitse zoweta zako ziri bwanji,Samalira magulu ako;

24. Pakuti cuma siciri cosatha;Kodi korona alipobe mpaka mibadwo mibadwo?

25. Amatuta maudzu, msipu uoneka,Achera masamba a kumapiri,

26. Ana a nkhosa akubveka,Atonde aombolera munda;

Werengani mutu wathunthu Miyambi 27