Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 27:1-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Usanyadire zamawa,Popeza sudziwa tsiku lina lidzabala ciani?

2. Wina akutame, si m'kamwamwako ai;Mlendo, si milomo ya iwe wekha.

3. Mwala ulemera, mcenga ndiwo katundu;Koma mkwiyo wa citsiru upambana kulemera kwace.

4. Kupweteka mtima nkwa nkhanza, mkwiyo usefuka;Koma ndani angalakike ndi nsanje?

5. Cidzudzulo comveka ciposa cikondi cobisika.

6. Kulasa kwa bwenzi kulikokhulupirika;Koma mdani apsompsona kawiri kawiri.

7. Mtima wokhuta upondereza cisa ca uci;Koma wakumva njala ayesa zowawa zonse zotsekemera.

8. Monga mbalame yosocera ku cisa cace,Momwemo munthu wosocera ku malo ace.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 27