1. Usanyadire zamawa,Popeza sudziwa tsiku lina lidzabala ciani?
2. Wina akutame, si m'kamwamwako ai;Mlendo, si milomo ya iwe wekha.
3. Mwala ulemera, mcenga ndiwo katundu;Koma mkwiyo wa citsiru upambana kulemera kwace.
4. Kupweteka mtima nkwa nkhanza, mkwiyo usefuka;Koma ndani angalakike ndi nsanje?
5. Cidzudzulo comveka ciposa cikondi cobisika.