Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 26:16-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Wolesi adziyesa wanzeruKoposa anthu asanu ndi awiri akuyankha mozindikira.

17. Wakungopita ndi kubvutika ndi ndeu yosakhala yaceAkunga wogwira makutu a garu.

18. Monga woyaruka woponya nsakali,Mibvi, ndi imfa,

19. Momwemo wonyenga mnzace ndi kuti, Ndi kusewera kumeneku.

20. Posowa nkhuni moto ungozima;Ndi popanda kazitape makangano angoleka.

21. Monga makala ozizira pa makala akunyeka, ndi nkhuni pamoto;Momwemo munthu wamakangano autsa ndeu.

22. Mau a kazitape ndi zakudya zolongosokaZitsikira m'kati mwa mimba.

23. Milomo yofunitsitsa ndi mtima woipaIkunga mbale yadothi anaimata ndi mphala yasiliva.

24. Wakuda mnzace amanyenga ndi milomo yace;Koma akundika cinyengo m'kati mwace;

25. Pamene akometsa mau ace usamkhulupirire;Pakuti m'mtima mwace muli zonyansa zisanu ndi ziwiri.

26. Angakhale abisa udani wace pocenjera,Koma udio wace udzabvumbulutsidwa posonkhana anthu.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 26