Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 26:11-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Monga garu abweranso ku masanzi ace,Momwemo citsiru cicitanso zopusa zace.

12. Kodi uona munthu wodziyesa wanzeru?Ngakhale citsiru cidzacenjera koma ameneyo ai.

13. Wolesi ati, Mkango uli panjira,Wobangulawo uli m'makwalala.

14. Monga citseko cikankhikira pa zitsulo za pamphuthu,Momwemo wolesi agubuduka pakama pace.

15. Wolesi alonga dzanja lace m'mbale;Kumtopetsa kulibweza kukamwa kwace.

16. Wolesi adziyesa wanzeruKoposa anthu asanu ndi awiri akuyankha mozindikira.

17. Wakungopita ndi kubvutika ndi ndeu yosakhala yaceAkunga wogwira makutu a garu.

18. Monga woyaruka woponya nsakali,Mibvi, ndi imfa,

19. Momwemo wonyenga mnzace ndi kuti, Ndi kusewera kumeneku.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 26