Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 26:1-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Monga cipale cofewa m'malimwe, ndi mvula m'masika,Momwemo ulemu suyenera citsiru.

2. Monga mpheta irikuzungulira, ndi namzeze alikuuluka,Momwemo temberero la pacabe silifikira.

3. Cikoti ciyenera kavalo, ndi cam'kamwa ciyenera buru,Ndi ntyole iyenera pamsana pa zitsiru.

4. Usayankhe citsiru monga mwa utsiru wace,Kuti ungafanane naco iwe wekha.

5. Yankha citsiru monga mwa utsiru wace,Kuti asadziyese wanzeru.

6. Wotumiza mau ndi dzanja la citsiruAdula mapazi ace, namwa zompweteka.

7. Miyendo ya wopunduka iri yolobodoka,Momwemo mwambi m'kamwa mwa zitsiru.

8. Monga thumba la ngale m'mulu wa miyala,Momwemo wocitira citsiru ulemu.

9. Monga munga wolasa dzanja la woledzera,Momwemo mwambi m'kamwa mwa zitsiru.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 26