Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 25:16-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Wapeza uci kodi? Idyapo wokwanira,Kuti ungakukole, nusanze.

17. Phazi lako lilowe m'nyumba ya mnzako kamodzi kamodzi;Kuti angatope nawe ndi kukuda.

18. Wocitira mnzace umboni wonamaNdiye cibonga, ndi lupanga, ndi mubvi wakuthwa.

19. Kukhulupirira munthu wa ciwembu tsiku latsokaKunga dzino lotyoka ndi phazi loguluka.

20. Monga wobvula maraya tsiku lamphepo,Ngakhale kuthira vinyo wosasa m'soda,Momwemo woyimbira nyimbo munthu wacisoni.

21. Mdani wako akamva njala umdyetse,Akamva ludzu ummwetse madzi,

22. Pakuti udzaunjika makala amoto pamtu pace;Ndipo Yehova adzakupatsa mphotho,

23. Mphepo ya kumpoto ifikitsa mvula;Comweco lilime losinjirira likwiyitsa nkhope.

24. Kukhala pa ngondya ya tsindwi kufunikaKuposa kukhala m'nyumba ndi mkazi wolongolola.

25. Monga madzi ozizira kwa munthu wotopa,Momwemo mau abwino akucokera ku dziko lakutari.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 25