Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 25:1-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Iyinso ndiyo miyambo ya SolomoImene anthu a Hezekiya mfumu ya Yuda anailemba.

2. Kubisa kanthu ndi ulemerero wa Mulungu;Koma ulemerero wa mafumu ndi kusanthula kanthu.

3. Pamlengalenga patarika, ndi padziko pakuya,Koma mitima ya mafumu singasanthulike.

4. Cotsera siliva mphala yace,Mmisiri wa ng'anjo aturutsamo mbale;

5. Cotsera woipa pamaso pa mfumu,Mpando wace udzakhazikika m'cilungamo.

6. Usadzitame pamaso pa mfumu,Ngakhale kuima m'malo mwa akuru;

7. Pakuti kunena kwa iwe, Takwera kuno,Kupambana ndi kuti utsitsidwe pamaso pa kalonga,Amene maso ako anamuona.

8. Usaturuke mwansontho kukalimbana,Ungalephere pa kutha kwace,Atakucititsa mnzako manyazi.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 25