28. Usacitire mnzako umboni womtsutsa opanda cifukwa;Kodi udzanyenga ndi milomo yako?
29. Usanene, Ndidzamcitira zomwezo anandicitira ine;Ndidzabwereza munthuyo monga mwa macitidwe ace.
30. Ndinapita pa munda wa wolesi,Polima mphesa munthu wosowa nzeru.
31. Taonani, ponsepo panamera minga,Ndi kuwirirapo khwisa;Chinga lace lamiyala ndi kupasuka.
32. Pamenepo ndinayang'ana ndi kuganizira,Ndinaona ndi kulandira mwambo.
33. Tulo tapang'ono, kungoodzera pang'ono,Kungomanga manja pang'ono m'kugona,
34. Ndipo umphawi wako udzafika ngati mbala;Ndi kusauka kwako ngati munthu wacikopa.