Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 24:26-34 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. Wobwezera mau oongokaApsompsona milomo.

27. Longosola nchito yako panjapo, nuikonzeretu kumunda;Pambuyo pace ndi kumanga nyumba yako.

28. Usacitire mnzako umboni womtsutsa opanda cifukwa;Kodi udzanyenga ndi milomo yako?

29. Usanene, Ndidzamcitira zomwezo anandicitira ine;Ndidzabwereza munthuyo monga mwa macitidwe ace.

30. Ndinapita pa munda wa wolesi,Polima mphesa munthu wosowa nzeru.

31. Taonani, ponsepo panamera minga,Ndi kuwirirapo khwisa;Chinga lace lamiyala ndi kupasuka.

32. Pamenepo ndinayang'ana ndi kuganizira,Ndinaona ndi kulandira mwambo.

33. Tulo tapang'ono, kungoodzera pang'ono,Kungomanga manja pang'ono m'kugona,

34. Ndipo umphawi wako udzafika ngati mbala;Ndi kusauka kwako ngati munthu wacikopa.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 24