19. Usabvutike mtima cifukwa ca ocita zoipa;Ngakhale kucitira nsanje amphulupulu;
20. Pakuti woipayo sadzalandira mphotho;Nyali ya amphulupulu idzazima.
21. Mwananga, opa Yehova ndi mfumu yomwe,Osadudukira anthu osinthasintha.
22. Pakuti tsoka lao lidzaoneka modzidzimuka;Ndipo ndani adziwa cionongeko ca zaka zao?
23. Izinso ziri za anzeru.Poweruza cetera siliri labwino.
24. Wonenakwa woipa, Wolungama iwe;Magulu a anthu adzamtemberera, mitundu ya anthu idzamkwiyira,
25. Omwe amdzudzula adzasekera,Nadzadalitsika ndithu.