17. Usakondwere pakugwa mdani wako;Mtima wako usasekere pokhumudwa iye;
18. Kuti Yehova angaone kukondwa kwako, ndi kukuyesa koipa,Ndi kuleka kumkwiyira.
19. Usabvutike mtima cifukwa ca ocita zoipa;Ngakhale kucitira nsanje amphulupulu;
20. Pakuti woipayo sadzalandira mphotho;Nyali ya amphulupulu idzazima.
21. Mwananga, opa Yehova ndi mfumu yomwe,Osadudukira anthu osinthasintha.
22. Pakuti tsoka lao lidzaoneka modzidzimuka;Ndipo ndani adziwa cionongeko ca zaka zao?
23. Izinso ziri za anzeru.Poweruza cetera siliri labwino.
24. Wonenakwa woipa, Wolungama iwe;Magulu a anthu adzamtemberera, mitundu ya anthu idzamkwiyira,
25. Omwe amdzudzula adzasekera,Nadzadalitsika ndithu.
26. Wobwezera mau oongokaApsompsona milomo.
27. Longosola nchito yako panjapo, nuikonzeretu kumunda;Pambuyo pace ndi kumanga nyumba yako.
28. Usacitire mnzako umboni womtsutsa opanda cifukwa;Kodi udzanyenga ndi milomo yako?
29. Usanene, Ndidzamcitira zomwezo anandicitira ine;Ndidzabwereza munthuyo monga mwa macitidwe ace.
30. Ndinapita pa munda wa wolesi,Polima mphesa munthu wosowa nzeru.
31. Taonani, ponsepo panamera minga,Ndi kuwirirapo khwisa;Chinga lace lamiyala ndi kupasuka.
32. Pamenepo ndinayang'ana ndi kuganizira,Ndinaona ndi kulandira mwambo.
33. Tulo tapang'ono, kungoodzera pang'ono,Kungomanga manja pang'ono m'kugona,
34. Ndipo umphawi wako udzafika ngati mbala;Ndi kusauka kwako ngati munthu wacikopa.