14. Potero udzadziwa kuti nzeru iri yotero m'moyo wako;Ngati waipeza padzakhala mphotho,Ndipo ciyembekezo cako sicidzalephereka.
15. Usabisalire, woipa iwe, pomanga wolungama;Usapasule popuma iyepo.
16. Pakuti wolungama amagwa kasanu ndi kawiri, nanyamukanso;Koma oipa akhumudwa pomfikira tsoka.
17. Usakondwere pakugwa mdani wako;Mtima wako usasekere pokhumudwa iye;
18. Kuti Yehova angaone kukondwa kwako, ndi kukuyesa koipa,Ndi kuleka kumkwiyira.
19. Usabvutike mtima cifukwa ca ocita zoipa;Ngakhale kucitira nsanje amphulupulu;
20. Pakuti woipayo sadzalandira mphotho;Nyali ya amphulupulu idzazima.
21. Mwananga, opa Yehova ndi mfumu yomwe,Osadudukira anthu osinthasintha.
22. Pakuti tsoka lao lidzaoneka modzidzimuka;Ndipo ndani adziwa cionongeko ca zaka zao?
23. Izinso ziri za anzeru.Poweruza cetera siliri labwino.