Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 24:14-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Potero udzadziwa kuti nzeru iri yotero m'moyo wako;Ngati waipeza padzakhala mphotho,Ndipo ciyembekezo cako sicidzalephereka.

15. Usabisalire, woipa iwe, pomanga wolungama;Usapasule popuma iyepo.

16. Pakuti wolungama amagwa kasanu ndi kawiri, nanyamukanso;Koma oipa akhumudwa pomfikira tsoka.

17. Usakondwere pakugwa mdani wako;Mtima wako usasekere pokhumudwa iye;

18. Kuti Yehova angaone kukondwa kwako, ndi kukuyesa koipa,Ndi kuleka kumkwiyira.

19. Usabvutike mtima cifukwa ca ocita zoipa;Ngakhale kucitira nsanje amphulupulu;

20. Pakuti woipayo sadzalandira mphotho;Nyali ya amphulupulu idzazima.

21. Mwananga, opa Yehova ndi mfumu yomwe,Osadudukira anthu osinthasintha.

22. Pakuti tsoka lao lidzaoneka modzidzimuka;Ndipo ndani adziwa cionongeko ca zaka zao?

23. Izinso ziri za anzeru.Poweruza cetera siliri labwino.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 24