1. Usacitire nsanje anthu oipa, Ngakhale kufuna kukhala nao;
2. Pakuti mtima wao ulingalira za cionongeko;Milomo yao ilankhula za mphulupulu.
3. Nzeru imangitsa nyumba;Luntha liikhazikitsa.
4. Kudziwa kudzaza zipinda zaceNdi cuma conse cofunika ca mtengo wace.
5. Mwamuna wanzeru ngwamphamvu;Munthu wodziwa ankabe nalimba.
6. Pakuti udzaponya nkhondo yako ndi upo,Ndi kupulumuka pocuruka aphungu,
7. Nzeru itarikira citsiru;Satsegula pakamwa kubwalo.
8. Wolingalira zakucita zoipaAnthu adzamcha waciwembu.