8. Pakuti nthongo imene unaidya udzaisanza,Ndi kutaya mau ako okondweretsa.
9. Usalankhule m'makutu a wopusa;Pakuti adzapeputsa nzeru ya mau ako.
10. Usasunthe cidziwitso cakale ca m'malire;Ngakhale kulowa m'minda ya amasiye;
11. Pakuti Mombolo wao walimba;Adzawanenera mlandu wao pa iwe.
12. Lozetsa mtima wako kumwambo,Ndi makutu ako ku mau a nzeru.