Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 23:7-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Pakuti monga asinkha m'kati mwace, ali wotere;Ati kwa iwe, Idya numwe;Koma mtima wace suli pa iwe.

8. Pakuti nthongo imene unaidya udzaisanza,Ndi kutaya mau ako okondweretsa.

9. Usalankhule m'makutu a wopusa;Pakuti adzapeputsa nzeru ya mau ako.

10. Usasunthe cidziwitso cakale ca m'malire;Ngakhale kulowa m'minda ya amasiye;

11. Pakuti Mombolo wao walimba;Adzawanenera mlandu wao pa iwe.

12. Lozetsa mtima wako kumwambo,Ndi makutu ako ku mau a nzeru.

13. Usamane mwana cilango;Pakuti ukammenya ndi ntyole safa ai.

14. Udzammenya ndi ntyole,Nudzapulumutsa moyo wace kunsi kwa manda.

15. Mwananga, mtima wako ukakhala wanzeru,Mtima wanga wa inedi udzakondwa;

16. Imso zanga zidzasangalala,Polankhula milomo yako zoongoka.

17. Mtima wako usacitire nsanje akucimwawo;Koma opabe Yehova tsiku lonse;

18. Pakutitu padzakhala mphotho;Ndipo ciyembekezo cako sicidzalephereka.

19. Tamvera tsopano, mwananga, utenge nzeru,Ulunjikitse mtima wako m'njiramo.

20. Usakhale mwa akumwaimwa vinyo,Ndi ankhuli osusuka.

21. Pakuti wakumwaimwa ndi wosusukayo adzasauka;Ndipo kusinza kudzabveka munthu nsanza.

22. Tamvera atate wako anakubala,Usapeputse amako atakalamba.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 23