Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 23:21-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Pakuti wakumwaimwa ndi wosusukayo adzasauka;Ndipo kusinza kudzabveka munthu nsanza.

22. Tamvera atate wako anakubala,Usapeputse amako atakalamba.

23. Gula ntheradi, osaigulitsa;Nzeru, ndi mwambo, ndi luntha.

24. Atate wa wolungama adzasekeradi;Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.

25. Atate wako ndi amako akondwere,Amako wakukubala asekere.

26. Mwananga, undipatse mtima wako,Maso ako akondwere ndi njira zanga,

27. Pakuti mkazi wadama ndiye dzenje lakuya;Ndipo mkazi waciwerewere ndiye mbuna yopapatiza.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 23