Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 23:17-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Mtima wako usacitire nsanje akucimwawo;Koma opabe Yehova tsiku lonse;

18. Pakutitu padzakhala mphotho;Ndipo ciyembekezo cako sicidzalephereka.

19. Tamvera tsopano, mwananga, utenge nzeru,Ulunjikitse mtima wako m'njiramo.

20. Usakhale mwa akumwaimwa vinyo,Ndi ankhuli osusuka.

21. Pakuti wakumwaimwa ndi wosusukayo adzasauka;Ndipo kusinza kudzabveka munthu nsanza.

22. Tamvera atate wako anakubala,Usapeputse amako atakalamba.

23. Gula ntheradi, osaigulitsa;Nzeru, ndi mwambo, ndi luntha.

24. Atate wa wolungama adzasekeradi;Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.

25. Atate wako ndi amako akondwere,Amako wakukubala asekere.

26. Mwananga, undipatse mtima wako,Maso ako akondwere ndi njira zanga,

27. Pakuti mkazi wadama ndiye dzenje lakuya;Ndipo mkazi waciwerewere ndiye mbuna yopapatiza.

28. Pakuti abisalira ngati wacifwamba,Nacurukitsa anthu a ciwembu.

29. Ndani ali ndi cisoni? ndani asauka? ndani ali ndi makangano?Ndani ang'ung'udza? ndani alasidwa cabe? ndani afiira maso?

30. Ngamene acedwa pali vinyo,Napita kukafunafuna vinyo wosanganizidwa.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 23