17. Mtima wako usacitire nsanje akucimwawo;Koma opabe Yehova tsiku lonse;
18. Pakutitu padzakhala mphotho;Ndipo ciyembekezo cako sicidzalephereka.
19. Tamvera tsopano, mwananga, utenge nzeru,Ulunjikitse mtima wako m'njiramo.
20. Usakhale mwa akumwaimwa vinyo,Ndi ankhuli osusuka.
21. Pakuti wakumwaimwa ndi wosusukayo adzasauka;Ndipo kusinza kudzabveka munthu nsanza.
22. Tamvera atate wako anakubala,Usapeputse amako atakalamba.
23. Gula ntheradi, osaigulitsa;Nzeru, ndi mwambo, ndi luntha.
24. Atate wa wolungama adzasekeradi;Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.
25. Atate wako ndi amako akondwere,Amako wakukubala asekere.
26. Mwananga, undipatse mtima wako,Maso ako akondwere ndi njira zanga,
27. Pakuti mkazi wadama ndiye dzenje lakuya;Ndipo mkazi waciwerewere ndiye mbuna yopapatiza.
28. Pakuti abisalira ngati wacifwamba,Nacurukitsa anthu a ciwembu.
29. Ndani ali ndi cisoni? ndani asauka? ndani ali ndi makangano?Ndani ang'ung'udza? ndani alasidwa cabe? ndani afiira maso?
30. Ngamene acedwa pali vinyo,Napita kukafunafuna vinyo wosanganizidwa.