Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 23:15-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Mwananga, mtima wako ukakhala wanzeru,Mtima wanga wa inedi udzakondwa;

16. Imso zanga zidzasangalala,Polankhula milomo yako zoongoka.

17. Mtima wako usacitire nsanje akucimwawo;Koma opabe Yehova tsiku lonse;

18. Pakutitu padzakhala mphotho;Ndipo ciyembekezo cako sicidzalephereka.

19. Tamvera tsopano, mwananga, utenge nzeru,Ulunjikitse mtima wako m'njiramo.

20. Usakhale mwa akumwaimwa vinyo,Ndi ankhuli osusuka.

21. Pakuti wakumwaimwa ndi wosusukayo adzasauka;Ndipo kusinza kudzabveka munthu nsanza.

22. Tamvera atate wako anakubala,Usapeputse amako atakalamba.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 23