Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 23:13-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Usamane mwana cilango;Pakuti ukammenya ndi ntyole safa ai.

14. Udzammenya ndi ntyole,Nudzapulumutsa moyo wace kunsi kwa manda.

15. Mwananga, mtima wako ukakhala wanzeru,Mtima wanga wa inedi udzakondwa;

16. Imso zanga zidzasangalala,Polankhula milomo yako zoongoka.

17. Mtima wako usacitire nsanje akucimwawo;Koma opabe Yehova tsiku lonse;

18. Pakutitu padzakhala mphotho;Ndipo ciyembekezo cako sicidzalephereka.

19. Tamvera tsopano, mwananga, utenge nzeru,Ulunjikitse mtima wako m'njiramo.

20. Usakhale mwa akumwaimwa vinyo,Ndi ankhuli osusuka.

21. Pakuti wakumwaimwa ndi wosusukayo adzasauka;Ndipo kusinza kudzabveka munthu nsanza.

22. Tamvera atate wako anakubala,Usapeputse amako atakalamba.

23. Gula ntheradi, osaigulitsa;Nzeru, ndi mwambo, ndi luntha.

24. Atate wa wolungama adzasekeradi;Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.

25. Atate wako ndi amako akondwere,Amako wakukubala asekere.

26. Mwananga, undipatse mtima wako,Maso ako akondwere ndi njira zanga,

Werengani mutu wathunthu Miyambi 23