Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 23:1-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pamene ukhala ulinkudya ndi mkuru,Zikumbukira ameneyo ali pamaso pako;

2. Nuike mpeni pakhosi pako,Ngati uli wadyera.

3. Usakhumbe zolongosoka zace;Pokhala zakudya zonyenga.

4. Usadzitopetse kuti ulemere;Leka nzeru yako yako.

5. Kodi upenyeranji cimene kulibe?Pakuti cuma cunera mapiko,Ngati mphungu youluka mumlengalenga.

6. Usadye zakudya zace za wa maso ankhwenzule,Ngakhale kukhumba zolongosoka zace;

7. Pakuti monga asinkha m'kati mwace, ali wotere;Ati kwa iwe, Idya numwe;Koma mtima wace suli pa iwe.

8. Pakuti nthongo imene unaidya udzaisanza,Ndi kutaya mau ako okondweretsa.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 23