Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 23:1-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pamene ukhala ulinkudya ndi mkuru,Zikumbukira ameneyo ali pamaso pako;

2. Nuike mpeni pakhosi pako,Ngati uli wadyera.

3. Usakhumbe zolongosoka zace;Pokhala zakudya zonyenga.

4. Usadzitopetse kuti ulemere;Leka nzeru yako yako.

5. Kodi upenyeranji cimene kulibe?Pakuti cuma cunera mapiko,Ngati mphungu youluka mumlengalenga.

6. Usadye zakudya zace za wa maso ankhwenzule,Ngakhale kukhumba zolongosoka zace;

7. Pakuti monga asinkha m'kati mwace, ali wotere;Ati kwa iwe, Idya numwe;Koma mtima wace suli pa iwe.

8. Pakuti nthongo imene unaidya udzaisanza,Ndi kutaya mau ako okondweretsa.

9. Usalankhule m'makutu a wopusa;Pakuti adzapeputsa nzeru ya mau ako.

10. Usasunthe cidziwitso cakale ca m'malire;Ngakhale kulowa m'minda ya amasiye;

11. Pakuti Mombolo wao walimba;Adzawanenera mlandu wao pa iwe.

12. Lozetsa mtima wako kumwambo,Ndi makutu ako ku mau a nzeru.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 23