Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 22:8-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Wofesa zosalungama adzakolola tsoka;Ndipo ntyole ya mkwiyo wace idzalephera.

9. Mwini diso lamataya adzadala;Pakuti apatsa osauka zakudya zace.

10. Ukainga wonyoza, makangano adzaturuka;Makani ndi manyazi adzalekeka.

11. Wokonda kuyera mtima,Mfumu idzakhala bwenzi lace cifukwa ca cisomo ca milomo yace.

12. Maso a Yehova acinjiriza wodziwa;Koma agwetsa mau a munthu wa ziwembu.

13. Waulesi ati, Pali mkango panjapo,Ndidzaphedwa pamakwalalapo.

14. M'kamwa mwa mkazi waciwerewere muli dzenje lakuya;Yemwe Yehova amkwiyira adzagwamo.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 22